< Masalimo 116 >

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
I love Yahweh—because he heareth my voice, my supplications;
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Because he hath bowed down his ear unto me, therefore, throughout my days, will I call.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
The meshes of death encompassed me, and the distresses of hades, came upon me, Peril and sorrow, I found; (Sheol h7585)
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
But, on the Name of Yahweh, I called—I beseech thee, Yahweh, deliver my soul.
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Gracious is Yahweh and righteous, and, our God, is full of compassion.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
Yahweh, preserveth the simple, I was brought low, when, to me, he granted salvation.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Return, O my soul, to thy rest, For, Yahweh, hath dealt bountifully with thee.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
For thou hast rescued my soul from death, —mine eyes from tears, my feet from stumbling.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
I will walk to and fro before Yahweh, in the lands of life.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
I believed that I should speak, I, was greatly depressed.
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
I, said in mine alarm, All men, are false!
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
How shall I give back to Yahweh, All his benefits unto me?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
The cup of salvation, will I lift, and, on the Name of Yahweh, will I call:
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
My vows—to Yahweh, will I pay, Might it be in presence of all his people!
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Costly in the eyes of Yahweh, is, death, for his men of lovingkindness.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
I beseech thee, O Yahweh—for, I, am thy servant, —I, am thy servant, the son of thy handmaid, Thou hast loosened my bonds.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
To thee, will I sacrifice a sacrifice of thanksgiving, and, on the Name of Yahweh, will I call:
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
My vows—to Yahweh, will I pay, Might it be in the presence of all his people; —
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
In the courts of the house of Yahweh, In the midst of thee, O Jerusalem. Praise ye Yah!

< Masalimo 116 >