< Masalimo 116 >
1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
I have loved, because YHWH hears My voice, my supplication,
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Because He has inclined His ear to me, And during my days I call.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
Cords of death have surrounded me, And straits of Sheol have found me, I find distress and sorrow. (Sheol )
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
And in the Name of YHWH I call: Ah, now, O YHWH, deliver my soul,
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
YHWH [is] gracious, and righteous, Indeed, our God [is] merciful,
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
YHWH [is] a preserver of the simple, I was low, and He gives salvation to me.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Return, O my soul, to your rest, For YHWH has conferred benefits on you.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
For You have delivered my soul from death, My eyes from tears, my feet from overthrowing.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
I habitually walk before YHWH In the lands of the living.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
I have believed, for I speak, I have been greatly afflicted.
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
I said in my haste, “Every man [is] a liar.”
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
What do I return to YHWH? All His benefits [are] on me.
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
I lift up the cup of salvation, And in the Name of YHWH I call.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
Let me complete my vows to YHWH, Now, before all His people.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Precious in the eyes of YHWH [is] the death of His saints.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
Ah, now, O YHWH, for I [am] Your servant; I [am] Your servant, son of Your handmaid; You have opened my bonds.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
I sacrifice a sacrifice of thanks to You, And in the Name of YHWH I call.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
Let me complete my vows to YHWH, Now, before all His people,
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
In the courts of the house of YHWH, In your midst, O Jerusalem, praise YAH!