< Masalimo 116 >
1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
I have loved, because the Lord will hear the voice of my prayer.
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Because he hath inclined his ear unto me: and in my days I will call upon him.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
The sorrows of death have encompassed me: and the perils of hell have found me. I met with trouble and sorrow: (Sheol )
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
And I called upon the name of the Lord. O Lord, deliver my soul.
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
The Lord is merciful and just, and our God sheweth mercy.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
The Lord is the keeper of little ones: I was little and he delivered me.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Turn, O my soul, into thy rest: for the Lord hath been bountiful to thee.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
For he hath delivered my soul from death: my eyes from tears, my feet from falling.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
I will please the Lord in the land of the living.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
I have believed, therefore have I spoken; but I have been humbled exceedingly.
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
I said in my excess: Every man is a liar.
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
What shall I render to the Lord, for all the things he hath rendered unto me?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
I will take the chalice of salvation; and I will call upon the name of the Lord.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
I will pay my vows to the Lord before all his people:
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Precious in the sight of the Lord is the death of his saints.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
O Lord, for I am thy servant: I am thy servant, and the son of thy handmaid. Thou hast broken my bonds:
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
I will sacrifice to thee the sacrifice of praise, and I will call upon the name of the Lord.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
I will pay my vows to the Lord in the sight of all his people:
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
In the courts of the house of the Lord, in the midst of thee, O Jerusalem.