< Masalimo 116 >

1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
Ik heb lief, want de HEERE hoort mijn stem, mijn smekingen;
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
Want Hij neigt Zijn oor tot mij; dies zal ik Hem in mijn dagen aanroepen.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol h7585)
De banden des doods hadden mij omvangen, en de angsten der hel hadden mij getroffen; ik vond benauwdheid en droefenis. (Sheol h7585)
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Maar ik riep den Naam des HEEREN aan, zeggende: Och HEERE! bevrijd mijn ziel.
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
De HEERE is genadig en rechtvaardig, en onze God is ontfermende.
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
De HEERE bewaart de eenvoudigen; ik was uitgeteerd, doch Hij heeft mij verlost.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Mijn ziel! keer weder tot uw rust, want de HEERE heeft aan u welgedaan.
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
Want Gij, HEERE! hebt mijn ziel gered van den dood, mijn ogen van tranen, mijn voet van aanstoot.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Ik zal wandelen voor het aangezicht des HEEREN, in de landen der levenden.
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
Ik heb geloofd, daarom sprak ik; ik ben zeer bedrukt geweest.
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
Ik zeide in mijn haasten: Alle mensen zijn leugenaars.
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
Wat zal ik den HEERE vergelden voor al Zijn weldaden aan mij bewezen?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
Ik zal den beker der verlossingen opnemen, en den Naam des HEEREN aanroepen.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
Mijn geloften zal ik den HEERE betalen, nu, in de tegenwoordigheid van al Zijn volk.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Kostelijk is in de ogen des HEEREN de dood Zijner gunstgenoten.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
Och, HEERE! zekerlijk ik ben Uw knecht, ik ben Uw knecht, een zoon Uwer dienstmaagd; Gij hebt mijn banden losgemaakt.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
Ik zal U offeren een offerande van dankzegging, en den Naam des HEEREN aanroepen.
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
Ik zal mijn gelofte den HEERE betalen, nu, in de tegenwoordigheid van al Zijn volk.
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
In de voorhoven van het huis des HEEREN, in het midden van u, o Jeruzalem! Hallelujah!

< Masalimo 116 >