< Masalimo 116 >
1 Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
Halleluja! Jeg elsker Herren, thi han hører min røst, min tryglende bøn,
2 Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
ja, han bøjed sit Øre til mig, jeg påkaldte HERRENs Navn.
3 Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
Dødens Bånd omspændte mig, Dødsrigets Angster greb mig, i Trængsel og Nød var jeg stedt. (Sheol )
4 Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
Jeg påkaldte HERRENs Navn: "Ak, HERRE, frels min Sjæl!"
5 Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
Nådig er HERREN og retfærdig, barmhjertig, det er vor Gud;
6 Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
HERREN vogter enfoldige, jeg var ringe, dog frelste han mig.
7 Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
Vend tilbage, min Sjæl, til din Ro, thi HERREN har gjort vel imod dig!
8 Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
Ja, han fried min Sjæl fra Døden, mit Øje fra Gråd, min Fod fra Fald.
9 kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
Jeg vandrer for HERRENs Åsyn udi de levendes Land;
10 Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
jeg troede, derfor talte jeg, såre elendig var jeg,
11 Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
sagde så i min Angst: "Alle Mennesker lyver!"
12 Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
Hvorledes skal jeg gengælde HERREN alle hans Velgerninger mod mig?
13 Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
Jeg vil løfte Frelsens Bæger og påkalde HERRENs Navn.
14 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
Jeg vil indfri HERREN mine Løfter i Påsyn af alt hans Folk.
15 Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
Kostbar i HERRENs Øjne er hans frommes Død.
16 Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
Ak, HERRE, jeg er jo din Tjener, din Tjener, din Tjenerindes Søn, mine Lænker har du løst.
17 Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
Jeg vil ofre dig Lovprisningsoffer og påkalde HERRENs Navn;
18 Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
mine Løfter vil jeg indfri HERREN i Påsyn af alt hans Folk
19 mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.
i HERRENs Hus's Forgårde og i din Midte, Jerusalem!