< Masalimo 115 >
1 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Ну ноуэ, Доамне, ну ноуэ, чи Нумелуй Тэу дэ славэ пентру бунэтатя Та, пентру крединчошия Та!
2 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
Пентру че сэ зикэ нямуриле: „Унде есте Думнезеул лор?”
3 Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
Думнезеул ностру есте ын чер, Ел фаче тот че вря.
4 Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Идолий лор сунт арӂинт ши аур, фэкуць де мынь оменешть.
5 Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
Ау гурэ, дар ну ворбеск; ау окь, дар ну вэд;
6 makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
ау урекь, дар н-ауд; ау нас, дар ну мирос;
7 manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
ау мынь, дар ну пипэе; пичоаре, дар ну мерг; ну скот ничун сунет дин гытлежул лор.
8 Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
Ка ей сунт чей че-й фак, тоць чей че се ынкред ын ей.
9 Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Исраеле, ынкреде-те ын Домнул! Ел есте ажуторул ши скутул лор.
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
Каса луй Аарон, ынкреде-те ын Домнул! Ел есте ажуторул ши скутул лор.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Чей че вэ темець де Домнул, ынкредеци-вэ ын Домнул! Ел есте ажуторул ши скутул лор.
12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
Домнул Шь-адуче аминте де ной. Ел ва бинекувынта: ва бинекувынта каса луй Исраел, ва бинекувынта каса луй Аарон,
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
ва бинекувынта пе чей че се тем де Домнул, пе чей мичь ши пе чей марь.
14 Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
Домнул сэ вэ ынмулцяскэ тот май мулт, пе вой ши пе копиий воштри!
15 Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Фиць бинекувынтаць де Домнул, каре а фэкут черуриле ши пэмынтул!
16 Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
Черуриле сунт але Домнулуй, дар пэмынтул л-а дат фиилор оаменилор.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
Ну морций лаудэ пе Домнул ши нич вреунул дин чей че се кобоарэ ын локул тэчерий,
18 ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.
чи ной, ной вом бинекувынта пе Домнул, де акум ши пынэ ын вяк. Лэудаць пе Домнул!