< Masalimo 115 >

1 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
KAIDIN kit Ieowa, kaidin kit, pwe mar omui, kom kotiki ong waui, pweki omui kalangan o melel!
2 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
Menda men liki kan en inda: Ia arail Kot?
3 Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
Atail Kot kotikot nanlang, a kak kotin wia karos, me a kupura.
4 Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Arail dikedik en ani kan, me wia kidar silper de kold, iei dodok en pa en aramas.
5 Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
Au arail mia, ap sasa lokaia, por en mas arail mia, ap sota kak kilang wasa;
6 makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
Salong arail mia, ap sota rong wasa; tum arail mia, ap sota ned wasa;
7 manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
Pa arail mia, ap sota kak koledi meakot; nä arail mia, ap sota kak alu; re sota kak lokaiaki kaping wor arail.
8 Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
Me kin wiada pukat, me dueta irail, o pil karos, me kin liki irail.
9 Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
A koe Israel, liki Ieowa; i sauas o pere parail.
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
Komail, kadaudok en Aron, liki Ieowa, i sauas o pere parail.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Komail, me kin masak Ieowa, liki Ieowa, i sauas o pere parail.
12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
Ieowa kotin kupura kitail er, o a pan kotin kapai kitail la; a pan kotin kapaida kadaudok en Israel, kapaida kadaudok en Aron;
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
A pan kotin kapaida, me masak Ieowa, me tikitik o me laud akan.
14 Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
Ieowa en kotin kapai komail da kokolata, pein komail o noumail seri kan!
15 Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Komail me kapaidar ren Ieowa, me kotin kapikadar lang o sappa.
16 Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
Lang me sapwilim en Ieowa, a sappa me a kotiki onger aramas akan.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
Me melar akan solar pan kapinga Ieowa, pil karos, me kodi wasan kaporemen;
18 ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.
A kitail pan kapinga Ieowa sang met o kokolata. Aleluia!

< Masalimo 115 >