< Masalimo 115 >
1 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Kakungabi kithi, Oh Thixo, hatshi kithi kodwa kwelakho ibizo kakube lenkazimulo, ngenxa yothando lokuthembeka Kwakho.
2 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
Kungani izizwe zisithi, “Ungaphi uNkulunkulu wabo na?”
3 Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
UNkulunkulu wethu usezulwini; wenza loba yini ayithandayo.
4 Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Kodwa izithombe zabo yisiliva legolide, zenziwe ngezandla zabantu.
5 Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
Zilemilomo, kodwa kazikhulumi, amehlo, kodwa kaziboni;
6 makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
zilezindlebe, kodwa kazizwa, amakhala, kodwa kazinuki lutho;
7 manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
zilezandla, kodwa kazenelisi ukuthinta, inyawo, kodwa kazihambi; njalo ngeke nje zenze umsindo ngemphimbo yazo.
8 Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
Labo abazenzayo bazakuba njengazo, kube njalo lakulabo abathemba kuzo.
9 Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Oh ndlu ka-Israyeli, methembe uThixo lusizo lwabo lesihlangu sabo.
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
Oh, ndlu ka-Aroni, methembe uThixo ulusizo lwabo lesihlangu sabo.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Lina elimesabayo, thembani kuThixo ulusizo lwabo lesihlangu sabo.
12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
UThixo uyasikhumbula njalo uzasibusisa: Uzayibusisa indlu ka-Israyeli, uzayibusisa indlu ka-Aroni,
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
uzababusisa labo abamesabayo uThixo abancinyane labakhulu ngokufananayo.
14 Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
Sengathi uThixo angalenza lande, lonke lina kanye labantwana benu.
15 Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Sengathi lingabusiswa nguThixo uMenzi wezulu lomhlaba.
16 Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
NgakaThixo amazulu aphezu kwakho konke, kodwa umhlaba wawunika abantu.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
Kakusibo abafileyo abadumisa uThixo, labo abangena phansi ekuthuleni;
18 ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.
yithi esimbabazayo uThixo, khona manje kanye laphakade. Dumisani uThixo.