< Masalimo 115 >
1 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Saan a kadakami, O Yahweh, saan a kadakami, ngem iti naganmo ti pangtedam iti pammadayaw, gapu iti kinapudnom iti tulagmo ken iti kinamatalekmo.
2 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
Apay koma nga ibaga dagiti nasion, “Sadino ti ayan ti Diosda?”
3 Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
Ti Diosmi ket adda sadi langit; ar-aramidenna ti aniaman a pagayatanna.
4 Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Pirak ken balitok dagiti didiosen dagiti pagilian nga aramid dagiti ima dagiti tattao.
5 Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
Addaan iti ngiwat dagitoy a didiosen, ngem saanda nga agsao; addaanda iti mata, ngem saanda a makakita;
6 makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
addaanda iti lapayag, ngem saanda a makangngeg; addaanda ti agung ngem saanda a makaangot;
7 manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
addaanda iti ima, ngem saanda a makarikna; addaanda iti saka, ngem saanda a makapagna, wenno agsao kadagiti ngiwatda.
8 Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
Dagiti nangaramid kadakuada ket kasla kadakuada, kasta met kadagiti amin nga agtaltalek kadakuada.
9 Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Israel, agtalekka kenni Yahweh; isuna ti tulong ken kalasagmo
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
Dakayo a sangkabalayan ni Aaron, agtalekkayo kenni Yahweh; isuna ti tulong ken kalasagyo.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Dakayo nga mangidaydayaw kenni Yahweh, agtalekkayo kenkuana; isuna ti tulong ken kalasagyo.
12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
Laglagipennatayo ni Yahweh ket bendisionannatayo; bendisionanna ti pamilia ti Israel; bendisionanna ti pamilia ni Aaron.
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
Bendisionanna dagiti mangraraem kenkuana, dagiti ubbing ken nataengan.
14 Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
Paadduennakayo koma ni Yahweh iti kasta unay, dakayo ken dagiti kaputotanyo.
15 Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Bendisionannakayo koma ni Yahweh, a nangaramid iti langit ken daga.
16 Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
Kukua ni Yahweh ti langit; ngem intedna ti lubong iti sangkataoan.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
Saan a dayawen dagiti natay ni Yahweh, wenno ti siasinoman a napanen iti kinaulimek.
18 ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.
Ngem idaydayawtayo ni Yahwen ita ken iti agnanayon. Idaydayawyo ni Yahweh.