< Masalimo 115 >
1 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Non point à nous, ô Eternel! non point à nous, mais à ton Nom donne gloire pour l'amour de ta miséricorde, pour l'amour de ta vérité.
2 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
Pourquoi diraient les nations: où est maintenant leur Dieu?
3 Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
Certes notre Dieu est aux cieux; il fait tout ce qu'il lui plaît.
4 Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Leurs dieux sont des [dieux] d'or et d'argent, un ouvrage des mains d'homme.
5 Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
Ils ont une bouche, et ne parlent point; ils ont des yeux, et ne voient point;
6 makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
Ils ont des oreilles, et n'entendent point; ils ont un nez, et ils n'[en] flairent point;
7 manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
Des mains, et ils n'[en] touchent point; des pieds, et ils n'en marchent point; [et] ils ne rendent aucun son de leur gosier.
8 Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
Que ceux qui les font, [et] tous ceux qui s'y confient, leur soient faits semblables.
9 Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Israël confie-toi en l'Eternel; il est le secours et le bouclier de ceux [qui se confient en lui].
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
Maison d'Aaron, confiez-vous en l'Eternel; il est leur aide et leur bouclier.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Vous qui craignez l'Eternel, confiez-vous en l'Eternel; il est leur aide et leur bouclier.
12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
L'Eternel s'est souvenu de nous, il bénira, il bénira la maison d'Israël, il bénira la maison d'Aaron.
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
Il bénira ceux qui craignent l'Eternel, tant les petits que les grands.
14 Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
L'Eternel ajoutera [bénédiction] sur vous, sur vous et sur vos enfants.
15 Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Vous êtes bénis de l'Eternel, qui a fait les cieux et la terre.
16 Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
Quant aux Cieux, les Cieux sont à l'Eternel; mais il a donné la terre aux enfants des hommes.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
Les morts, et tous ceux qui descendent où l'on ne dit plus mot, ne loueront point l'Eternel.
18 ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.
Mais nous, nous bénirons l'Eternel dès maintenant, et à toujours. Louez l'Eternel.