< Masalimo 115 >

1 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Non point à nous, ô Éternel! non point à nous, mais à ton nom donne gloire, à cause de ta bonté, à cause de ta vérité.
2 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
Pourquoi les nations diraient-elles: Où donc est leur Dieu?
3 Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
Mais notre Dieu est aux cieux; tout ce qu’il lui a plu, il l’a fait.
4 Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Leurs idoles sont de l’argent et de l’or, ouvrage de mains d’homme:
5 Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
Elles ont une bouche et ne parlent pas; elles ont des yeux et ne voient pas;
6 makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
Elles ont des oreilles et n’entendent pas; elles ont un nez et ne sentent pas;
7 manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
Elles ont des mains et ne touchent pas; des pieds, et ne marchent pas; elles ne rendent aucun son de leur gosier.
8 Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
Ceux qui les ont faites, tous ceux qui se confient en elles, sont comme elles.
9 Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Israël, confie-toi en l’Éternel: il est leur secours et leur bouclier.
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
Maison d’Aaron, confiez-vous en l’Éternel: il est leur secours et leur bouclier.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Vous qui craignez l’Éternel, confiez-vous en l’Éternel: il est leur secours et leur bouclier.
12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
L’Éternel s’est souvenu de nous: il bénira, il bénira la maison d’Israël; il bénira la maison d’Aaron;
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
Il bénira ceux qui craignent l’Éternel, les petits avec les grands.
14 Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
L’Éternel vous augmentera [sa bénédiction], à vous et à vos fils.
15 Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Vous êtes bénis de l’Éternel, qui a fait les cieux et la terre.
16 Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
Les cieux sont les cieux de l’Éternel, mais il a donné la terre aux fils des hommes.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
Ni les morts, ni tous ceux qui descendent dans le silence, ne loueront Jah.
18 ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.
Mais nous, nous bénirons Jah, dès maintenant et à toujours. Louez Jah!

< Masalimo 115 >