< Masalimo 115 >

1 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Not to us, O YHWH, not to us, But to Your Name give glory, For Your kindness, for Your truth.
2 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
Why do the nations say, “Where, pray, [is] their God?”
3 Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
And our God [is] in the heavens, All that He has pleased He has done.
4 Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Their idols [are] silver and gold, work of man’s hands,
5 Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
They have a mouth, and they do not speak, They have eyes, and they do not see,
6 makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
They have ears, and they do not hear, They have a nose, and they do not smell,
7 manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
Their hands, but they do not handle, Their feet, and they do not walk;
8 Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
Nor do they mutter through their throat, Their makers are like them, Everyone who is trusting in them.
9 Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
O Israel, trust in YHWH, “He [is] their help and their shield.”
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
O house of Aaron, trust in YHWH, “He [is] their help and their shield.”
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
You fearing YHWH, trust in YHWH, “He [is] their help and their shield.”
12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
YHWH has remembered us, He blesses, He blesses the house of Israel, He blesses the house of Aaron,
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
He blesses those fearing YHWH, The small with the great.
14 Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
YHWH adds to you—to you and to your sons.
15 Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Blessed [are] you of YHWH, Maker of the heavens and earth,
16 Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
The heavens—the heavens [are] YHWH’s, And He has given the earth to sons of men;
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
The dead do not praise YAH, Nor any going down to silence.
18 ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.
And we, we bless YAH, From now on, and for all time. Praise YAH!

< Masalimo 115 >