< Masalimo 115 >

1 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Not to us, O Lord, not to us, but to thy name give glory, because of thy mercy and thy truth;
2 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
lest at any time the nations should say, Where is their God?
3 Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
But our God has done in heaven and on earth, whatsoever he has pleased.
4 Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
The idols of the nations are silver and gold, the works of men's hands.
5 Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
They have a mouth, but they cannot speak; they have eyes, but they cannot see:
6 makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
they have ears, but they cannot hear; they have noses, but they cannot smell;
7 manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
they have hands, but they cannot handle; they have feet, but they cannot walk: they cannot speak through their throat.
8 Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
Let those that make them become like to them, and all who trust in them.
9 Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
The house of Israel trusts in the Lord: he is their helper and defender.
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
The house of Aaron trusts in the Lord: he is their helper and defender.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
They that fear the Lord trust in the Lord: he is their helper and defender.
12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
The Lord has remembered us, and blessed us: he has blessed the house of Israel, he has blessed the house of Aaron.
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
He has blessed them that fear the Lord, both small and great.
14 Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
The Lord add [blessings] to you and to your children.
15 Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Blessed are ye of the Lord, who made the heaven and the earth.
16 Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
The heaven of heavens [belongs] to the Lord: but he has given the earth to the sons of men.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
The dead shall not praise thee, O Lord, nor any that go down to Hades.
18 ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.
But we, the living, will bless the Lord, from henceforth and for ever.

< Masalimo 115 >