< Masalimo 115 >

1 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
Ne nám, Hospodine, ne nám, ale jménu svému dej čest, pro milosrdenství své a pro pravdu svou.
2 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
Proč mají říkati pohané: Kdež jest nyní Bůh jejich?
3 Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
Ješto Bůh náš jest na nebi, čině všecko, což se mu líbí.
4 Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Modly pak jejich jsou stříbro a zlato, dílo rukou lidských.
5 Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
Ústa mají, a nemluví, oči mají, a nevidí.
6 makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
Uši mají, a neslyší, nos mají, a nečijí.
7 manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
Ruce mají, a nemakají, nohy mají, a nechodí, aniž volati mohou hrdlem svým.
8 Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
Nechať jsou jim podobni, kteříž je dělají, a kdožkoli v nich doufají.
9 Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Izraeli, doufej v Hospodina, nebo spomocníkem a štítem takových on jest.
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
Dome Aronův, doufej v Hospodina, spomocníkem a štítem takových on jest.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Kteříž se bojíte Hospodina, doufejte v Hospodina, spomocníkem a štítem takových on jest.
12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
Hospodin rozpomena se na nás, požehná; požehná domu Izraelovu, požehná i domu Aronovu.
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
Požehná bojícím se Hospodina, malým, i velikým.
14 Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
Rozmnoží Hospodin vás, vás i syny vaše.
15 Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Požehnaní vy od Hospodina, kterýž učinil nebesa i zemi.
16 Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
Nebesa jsou nebesa Hospodinova, zemi pak dal synům lidským.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
Ne mrtví chváliti budou Hospodina, ani kdo ze všech těch, kteříž sstupují do místa mlčení,
18 ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.
Ale my dobrořečiti budeme Hospodinu od tohoto času až na věky. Halelujah.

< Masalimo 115 >