< Masalimo 115 >
1 Kwa ife ayi Yehova, kwa ife ayi koma ulemerero ukhale pa dzina lanu, chifukwa cha chikondi chanu chosasinthika ndiponso chifukwa cha kukhulupirika kwanu.
BOEIPA aw kaimih ham moenih. Kaimih ham pawt dae namah ming ham mah na sitlohnah, na uepomnah rhang neh thangpomnah te pae lah.
2 Chifukwa chiyani anthu a mitundu ina akunena kuti, “Mulungu wawo ali kuti?”
Ba dongah lae namtom rhoek loh, “A Pathen khaw melae me?,” a ti uh.
3 Mulungu wathu ali kumwamba; Iye amachita chilichonse chimene chimamukondweretsa.
Tedae kaimih kah Pathen tah vaan ah om tih, amah loh a ngaih te boeih a saii.
4 Koma mafano awo ndi siliva ndi golide, opangidwa ndi manja a anthu.
Amih kah muei rhoek ngawntah cak neh sui neh hlang kut long ni a bi.
5 Pakamwa ali napo koma sayankhula, maso ali nawo koma sapenya;
Amih te a ka om dae cal uh thai pawh. A mik te om dae hmuh uh thai pawh.
6 makutu ali nawo koma samva, mphuno ali nazo koma sanunkhiza;
A hna te om dae ya uh pawh. A hnarhong te om dae him uh thai pawh.
7 manja ali nawo koma akakhudza samva kanthu; mapazi ali nawo koma sayenda; kapena pakhosi pawo kutulutsa mawu.
A kut om dae yam thai pawh. A kho om dae cet uh thai pawh. A olrhong neh cai uh thai pawh.
8 Anthu amene amapanga mafanowo adzafanana nawo, chimodzimodzinso onse amene amadalira mafanowo.
Amih aka saii tih amih dongah aka pangtung rhoek boeih khaw amih bangla pawtlawt om uh.
9 Inu Aisraeli, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
Israel na BOEIPA dongah pangtung lah. Amah te amih kah bomkung neh photling ni.
10 Iwe nyumba ya Aaroni, dalira Yehova; Iye ndiye thandizo lako ndi chishango chako.
Aaron imkhui nang BOEIPA dongah pangtung uh lah. Amah te amih kah bomkung neh photling ni.
11 Inu amene mumaopa Iye, dalirani Yehova; Iye ndiye thandizo lanu ndi chishango chanu.
BOEIPA aka rhih rhoek, BOEIPA dongah pangtung uh lah. Amah te amih kah bomkung neh photling ni.
12 Yehova watikumbukira ndipo adzatidalitsa: adzadalitsa nyumba ya Israeli, adzadalitsa nyumba ya Aaroni,
BOEIPA loh mamih he n'ngaidam. Israel imkhui he yoethen a paek a paek vetih Aron imkhui khaw yoethen a paek ni.
13 adzadalitsa iwo amene amaopa Yehova; aangʼono ndi aakulu omwe.
BOEIPA aka rhih tanoe kangham taengah yoethen a paek ni.
14 Yehova akuwonjezereni madalitso; inuyo pamodzi ndi ana anu.
BOEIPA loh nang neh na ca rhoek taengah hang koei saeh.
15 Mudalitsidwe ndi Yehova, Wolenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Vaan neh diklai aka saii BOEIPA loh nangmih yoethen m'paek coeng.
16 Kumwamba ndi kwa Yehova, koma dziko lapansi Iye walipereka kwa anthu.
Vaan vaan rhoek BOEIPA hut dae diklai he hlanghing koca taengah a paek.
17 Si anthu akufa amene amatamanda Yehova, amene amatsikira kuli chete;
Aka duek rhoek neh tuihoeng la aka suntla boeih BOEIPA a thangthen uh moenih.
18 ndi ife amene timatamanda Yehova, kuyambira tsopano mpaka muyaya. Tamandani Yehova.
Tedae mamih loh tahae lamkah kumhal due khaw BOEIPA uem uh sih. BOEIPA thangthen uh.