< Masalimo 114 >
1 Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
Як виходив Ізраїль з Єгипту, від наро́ду чужого дім Яковів, —
2 Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
Юда став за святиню Йому, а Ізраїль — Його панува́нням!
3 Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
Побачило море все це — і побі́гло, Йорда́н повернувся наза́д!
4 mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
Го́ри скака́ли, немов баранці́, а пагі́рки — немов ті ягня́та!
5 Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
Що́ тобі, море, що ти втікаєш? Йорда́не, що ти поверну́вся наза́д?
6 inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
Чого ска́чете, гори, немов баранці́, а па́гірки — мов ті ягня́та?
7 Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
Тремти, зе́мле, перед Господнім лицем, перед лицем Бога Якова,
8 amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.
що скелю обе́ртає в озеро водне, а кремінь — на водне джере́ло!