< Masalimo 114 >

1 Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
Alleluia. In exitu Israel de Aegypto, domus Iacob de populo barbaro:
2 Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
Facta est Iudaea sanctificatio eius, Israel potestas eius.
3 Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
Mare vidit, et fugit: Iordanis conversus est retrorsum.
4 mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
Montes exultaverunt ut arietes: et colles sicut agni ovium.
5 Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
Quid est tibi mare quod fugisti: et tu Iordanis, quia conversus es retrorsum?
6 inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
Montes exultastis sicut arietes, et colles sicut agni ovium?
7 Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
A facie Domini mota est terra, a facie Dei Iacob.
8 amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.
Qui convertit petram in stagna aquarum, et rupem in fontes aquarum.

< Masalimo 114 >