< Masalimo 114 >

1 Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
Quand Israël sortit d’Égypte, Quand la maison de Jacob s’éloigna d’un peuple barbare,
2 Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
Juda devint son sanctuaire, Israël fut son domaine.
3 Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
La mer le vit et s’enfuit, Le Jourdain retourna en arrière;
4 mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
Les montagnes sautèrent comme des béliers, Les collines comme des agneaux.
5 Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
Qu’as-tu, mer, pour t’enfuir, Jourdain, pour retourner en arrière?
6 inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
Qu’avez-vous, montagnes, pour sauter comme des béliers, Et vous, collines, comme des agneaux?
7 Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
Tremble devant le Seigneur, ô terre! Devant le Dieu de Jacob,
8 amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.
Qui change le rocher en étang, Le roc en source d’eaux.

< Masalimo 114 >