< Masalimo 114 >
1 Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
Alléluiah! Lorsque Israël sortit d'Egypte, et la maison de Jacob d'un peuple barbare,
2 Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
Juda devint son peuple saint, Israël sa puissance.
3 Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
La mer le vit, et s'enfuit; le Jourdain retourna en arrière.
4 mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
Les montagnes bondirent comme des béliers, et les collines comme des agneaux.
5 Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
Qu'avais-tu en toi, ô mer, pour fuir ainsi, et toi, Jourdain, pour retourner en arrière?
6 inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
Et vous, montagnes, pourquoi bondissiez-vous comme des béliers, et vous, collines, comme des agneaux?
7 Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
La terre a tremblé à la face du Seigneur, à la face du Dieu de Jacob,
8 amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.
Qui a changé la pierre en nappes d'eau, et la roche en fontaines.