< Masalimo 114 >

1 Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
When Israel [God prevails] went out of Egypt [Abode of slavery], the house of Jacob [Supplanter] from a people of foreign language;
2 Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
Judah [Praised] became his sanctuary, Israel [God prevails] his dominion.
3 Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
The sea saw it, and fled. The Jordan [Descender] was driven back.
4 mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
The mountains skipped like rams, the little hills like lambs.
5 Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
What was it, you sea, that you fled? You Jordan [Descender], that you turned back?
6 inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
You mountains, that you skipped like rams; you little hills, like lambs?
7 Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
Tremble, you earth, at the presence of the Lord, at the presence of the God of Jacob [Supplanter],
8 amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.
who turned the rock into a pool of water, the flint into a spring of waters.

< Masalimo 114 >