< Masalimo 114 >

1 Pamene Israeli anatuluka mu Igupto, nyumba ya Yakobo kuchoka ku mtundu wa anthu a chiyankhulo chachilendo,
Toen Israel uit Egypte toog, het huis Jakobs van een volk, dat een vreemde taal had;
2 Yuda anasanduka malo opatulika a Mulungu, Israeli anasanduka ufumu wake.
Zo werd Juda tot Zijn heiligdom, Israel Zijn volkomene heerschappij.
3 Nyanja inaona ndi kuthawa, mtsinje wa Yorodani unabwerera mʼmbuyo;
De zee zag het, en vlood; de Jordaan keerde achterwaarts.
4 mapiri analumphalumpha ngati nkhosa zazimuna, timapiri ngati ana ankhosa.
De bergen sprongen als rammen, de heuvelen als lammeren.
5 Nʼchifukwa chiyani iwe unathawa? iwe mtsinje wa Yorodani unabwereranji mʼmbuyo?
Wat was u, gij zee! dat gij vloodt? gij Jordaan! dat gij achterwaarts keerdet?
6 inu mapiri, munalumphalumphiranji ngati nkhosa zazimuna, inu timapiri, ngati ana ankhosa?
Gij bergen, dat gij opsprongt als rammen? gij heuvelen! als lammeren?
7 Njenjemera pamaso pa Ambuye iwe dziko lapansi, pamaso pa Mulungu wa Yakobo,
Beef, gij aarde! voor het aangezicht des Heeren, voor het aangezicht van den God Jakobs;
8 amene anasandutsa thanthwe kukhala chitsime, thanthwe lolimba kukhala akasupe a madzi.
Die den rotssteen veranderde in een watervloed, den keisteen in een waterfontein.

< Masalimo 114 >