< Masalimo 113 >

1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
Хвалите, слуге Господње, хвалите име Господње,
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Да буде име Господње благословено одсад и довека.
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
Од истока сунчаног до запада да се слави име Господње.
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
Узвишен је над свима народима Господ; сврх небеса је слава Његова.
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
Ко је као Господ, Бог наш, који седи на висини;
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
Који се сагиба да види шта је на небесима и на земљи;
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
Који из праха подиже убогога, и из кала узвишује ништега;
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
И посађује га с кнезовима, с кнезовима у народу његовом;
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
Од нероткиње насељава кућу, учинивши је радосном мајком синовима. Алилуја!

< Masalimo 113 >