< Masalimo 113 >

1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
Hvalite, sluge Gospodnje, hvalite ime Gospodnje,
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Da bude ime Gospodnje blagosloveno otsad i dovijeka.
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
Od istoka sunèanoga do zapada da se slavi ime Gospodnje.
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
Uzvišen je nad svima narodima Gospod; svrh nebesa je slava njegova.
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
Ko je kao Gospod, Bog naš, koji sjedi na visini;
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
Koji se sagiba da vidi što je na nebesima i na zemlji;
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
Koji iz praha podiže ubogoga, i iz kala uzvišuje ništega;
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
I posaðuje ga s knezovima, s knezovima u narodu njegovu;
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
Od nerotkinje naseljava kuæu, uèinivši je radosnom majkom sinovima. Aliluja!

< Masalimo 113 >