< Masalimo 113 >

1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
Aleluia! Louvai, vós servos do SENHOR, louvai o nome do SENHOR.
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Seja o nome do SENHOR bendito, desde agora para todo o sempre.
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
Desde o nascer do sol até o poente, seja louvado o nome do SENHOR.
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
O SENHOR está elevado acima de todas as nações; [e] sua glória acima dos céus.
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
Quem é como o SENHOR nosso Deus? Ele que habita nas alturas,
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
Que se abaixa para ver [o que há] nos céus e na terra;
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
Que do levanta o pobre do pó da terra, e levanta o necessitado da sujeira;
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
Para fazê-lo sentar com os príncipes, com os príncipes de seu povo;
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
Que faz a estéril habitar em família, como alegre mãe de filhos. Aleluia!

< Masalimo 113 >