< Masalimo 113 >

1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
Alleluja. [Laudate, pueri, Dominum; laudate nomen Domini.
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Sit nomen Domini benedictum ex hoc nunc et usque in sæculum.
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
A solis ortu usque ad occasum laudabile nomen Domini.
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
Excelsus super omnes gentes Dominus, et super cælos gloria ejus.
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
Quis sicut Dominus Deus noster, qui in altis habitat,
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
et humilia respicit in cælo et in terra?
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
Suscitans a terra inopem, et de stercore erigens pauperem:
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
ut collocet eum cum principibus, cum principibus populi sui.
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
Qui habitare facit sterilem in domo, matrem filiorum lætantem.]

< Masalimo 113 >