< Masalimo 113 >

1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
主をほめたたえよ。主のしもべたちよ、ほめたたえよ。主のみ名をほめたたえよ。
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
今より、とこしえに至るまで主のみ名はほむべきかな。
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
日のいずるところから日の入るところまで、主のみ名はほめたたえられる。
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
主はもろもろの国民の上に高くいらせられ、その栄光は天よりも高い。
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
われらの神、主にくらぶべき者はだれか。主は高き所に座し、
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
遠く天と地とを見おろされる。
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
主は貧しい者をちりからあげ、乏しい者をあくたからあげて、
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
もろもろの君たちと共にすわらせ、その民の君たちと共にすわらせられる。
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
また子を産まぬ女に家庭を与え、多くの子供たちの喜ばしい母とされる。主をほめたたえよ。

< Masalimo 113 >