< Masalimo 113 >
1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
ヱホバをほめまつれ汝等ヱホバの僕よほめまつれヱホバの名をほめまつれ
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
今より永遠にいたるまでヱホバの名はほむべきかな
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
日のいづる處より日のいる處までヱホバの名はほめらるべし
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
ヱホバはもろもろの國の上にありてたかく その榮光は天よりもたかし
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
われらの神ヱホバにたぐふべき者はたれぞや 寳座をその高處にすゑ己をひくくして天と地とをかへりみ給ふ
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
われらの神ヱホバにたぐふべき者はたれぞや 寳座をその高處にすゑ己をひくくして天と地とをかへりみ給ふ
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
まづしきものを塵よりあげ乏しきものを糞土よりあげて
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
もろもろの諸侯とともにすわらせ その民のきみたちと共にすわらせたまはん
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
又はらみなき婦に家をまもらせ おほくの子女のよろこばしき母たらしめたまふ ヱホバを讃まつれ