< Masalimo 113 >

1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
Louez le Seigneur, enfants, louez le nom du Seigneur.
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Soit le nom du Seigneur béni, dès ce moment et jusqu’à jamais.
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
Du lever du soleil jusqu’à son coucher, louable est le nom du Seigneur.
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
Il est élevé au-dessus de toutes les nations, le Seigneur, et au-dessus des cieux est sa gloire.
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
Qui est comme le Seigneur notre Dieu, qui habite dans les lieux les plus élevés,
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
Et regarde les choses basses dans le ciel et sur la terre?
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
Qui tire de la terre l’homme sans ressource, et qui relève du fumier le pauvre;
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
Afin de le placer avec des princes, avec les princes de son peuple.
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
Qui fait habiter la femme stérile dans une maison où il lui donne la joie d’être mère de plusieurs enfants.

< Masalimo 113 >