< Masalimo 113 >

1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
Alléluia! Louez, serviteurs de l’Eternel, louez le nom de l’Eternel!
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Que le nom du Seigneur soit béni dès maintenant et à tout jamais!
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
Du soleil levant jusqu’à son couchant, que le nom de l’Eternel soit célébré!
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
L’Eternel est élevé au-dessus de tous les peuples, sa gloire dépasse les cieux.
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
Qui, comme l’Eternel, notre Dieu, réside dans les hauteurs,
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
abaisse ses regards sur le ciel et sur la terre?
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
Il redresse l’humble couché dans la poussière, fait remonter le pauvre du sein de l’abjection,
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
pour le placer à côté des grands, à côté des grands de son peuple.
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
Il fait trôner dans la maison la femme stérile, devenue une mère heureuse de nombreux fils. Alléluia!

< Masalimo 113 >