< Masalimo 113 >

1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
Praise ye the LORD. Praise, O ye servants of the LORD, praise the name of the LORD.
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Blessed be the name of the LORD from this time forth and for evermore.
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
From the rising of the sun unto the going down of the same the LORD’s name [is] to be praised.
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
The LORD [is] high above all nations, [and] his glory above the heavens.
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
Who [is] like unto the LORD our God, who dwelleth on high,
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
Who humbleth [himself] to behold [the things that are] in heaven, and in the earth!
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
He raiseth up the poor out of the dust, [and] lifteth the needy out of the dunghill;
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
That he may set [him] with princes, [even] with the princes of his people.
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
He maketh the barren woman to keep house, [and to be] a joyful mother of children. Praise ye the LORD.

< Masalimo 113 >