< Masalimo 113 >

1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
Hallelujah! Praise, ye servants of Jehovah, praise the name of Jehovah.
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Blessed be the name of Jehovah, from this time forth and for evermore!
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
From the rising of the sun unto the going down of the same, let Jehovah's name be praised.
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
Jehovah is high above all nations, his glory above the heavens.
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
Who is like unto Jehovah our God, who hath placed his dwelling on high;
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
Who humbleth himself to look on the heavens and on the earth?
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
He raiseth up the poor out of the dust; from the dung-hill he lifteth up the needy,
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
To set [him] among nobles, among the nobles of his people.
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
He maketh the barren woman to keep house, [as] a joyful mother of sons. Hallelujah!

< Masalimo 113 >