< Masalimo 113 >
1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
Alleluia. Praise the Lord, ye servants [of his], praise, the name of the Lord.
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Let the name of the Lord be blessed, from this present time and for ever.
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
From the rising of the sun to his setting, the name of the Lord is to be praised.
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
The Lord is high above all the nations; his glory is above the heavens.
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
Who is as the Lord our God? who dwells in the high places,
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
and [yet] looks upon the low things in heaven, and on the earth:
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
who lifts up the poor from the earth, and raises up the needy from the dunghill;
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
to set him with princes, [even] with the princes of his people:
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
who settles the barren [woman] in a house, [as] a mother rejoicing over children.