< Masalimo 113 >

1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
Lover, I Herrens Tjenere, lover Herrens Navn!
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Lovet være Herrens Navn fra nu og indtil evig Tid!
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
Fra Solens Opgang indtil dens Nedgang er Herrens Navn højlovet.
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
Herren er høj over alle Hedninger, hans Herlighed er over Himlene.
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
Hvo er som Herren vor Gud? han, som har sat sit Sæde højt;
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
han, som stiger dybt ned for at se, i Himlene og paa Jorden;
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
han, som oprejser den ringe af Støvet, som ophøjer en fattig af Skarnet
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
for at sætte ham hos Fyrster, hos sit Folks Fyrster;
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
han, som gør, at den ufrugtbare i Huset kommer til at bo som en glad Barnemoder. Halleluja.

< Masalimo 113 >