< Masalimo 113 >
1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
Halelujah. Chvalte služebníci Hospodinovi, chvalte jméno Hospodinovo.
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
Budiž jméno Hospodinovo požehnáno od tohoto času až na věky.
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
Od východu slunce až do západu jeho chváleno buď jméno Hospodinovo.
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
Vyvýšenť jest nade všecky národy Hospodin, a nad nebesa sláva jeho.
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
Kdo jest rovný Hospodinu Bohu našemu, kterýž vysoko bydlí?
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
Kterýž snižuje se, aby všecko spatřoval, což jest na nebi i na zemi.
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
Vyzdvihuje z prachu nuzného, a z hnoje vyvyšuje chudého,
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
Aby jej posadil s knížaty, s knížaty lidu svého.
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
Kterýž vzdělává neplodnou v čeled, a matku veselící se z dítek. Halelujah.