< Masalimo 113 >

1 Tamandani Yehova. Mutamandeni, inu atumiki a Yehova, tamandani dzina la Yehova.
阿肋路亞!上主的僕人,請一齊讚頌,請一齊讚頌上主聖名!
2 Yehova atamandidwe, kuyambira tsopano mpaka muyaya.
願上主的名受讚頌,從現在直到永遠無窮!
3 Kuyambira ku matulukiro a dzuwa mpaka ku malowero ake, dzina la Yehova liyenera kutamandidwa.
從太陽東升到西落,願上主的聖名受讚頌!
4 Yehova wakwezeka pa anthu a mitundu yonse, ulemerero wake ndi woposa mayiko akumwamba.
上主高越列國萬邦;上主的光榮凌駕穹蒼;
5 Ndani wofanana ndi Yehova Mulungu wathu, Iye amene amakhala mwaufumu mmwamba?
誰能相似上主我們的天主?祂坐在蒼天之上的最高處。
6 amene amawerama pansi kuyangʼana miyamba ndi dziko lapansi?
上主必會垂目下視,觀看上天和下地;
7 Iye amakweza munthu wosauka kuchoka pa fumbi ndi kutukula munthu wosowa kuchoka pa dzala;
上主從塵埃裏提拔弱小的人;上主由糞土中舉揚窮苦的人,
8 amawakhazika pamodzi ndi mafumu, pamodzi ndi mafumu a anthu ake.
叫他與貴族的人共席,也與本國的王侯同位;
9 Amakhazikitsa mayi wosabereka mʼnyumba yake monga mayi wa ana wosangalala. Tamandani Yehova.
使那不孕的婦女坐鎮家中,成為多子的母親快樂無窮。

< Masalimo 113 >