< Masalimo 112 >
1 Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
Övgüler sunun RAB'be! Ne mutlu RAB'den korkan insana, O'nun buyruklarından büyük zevk alana!
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
Soyu yeryüzünde güç kazanacak, Doğruların kuşağı kutsanacak.
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Bolluk ve zenginlik eksilmez evinden, Sonsuza dek sürer doğruluğu.
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
Karanlıkta ışık doğar dürüstler için, Lütfeden, sevecen, doğru insanlar için.
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
Ne mutlu eli açık olan, ödünç veren, İşlerini adaletle yürüten insana!
6 Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
Asla sarsılmaz, Sonsuza dek anılır doğru insan.
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
Kötü haberden korkmaz, Yüreği sarsılmaz, RAB'be güvenir.
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
Gözü pektir, korku nedir bilmez, Sonunda düşmanlarının yenilgisini görür.
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
Armağanlar dağıttı, yoksullara verdi; Doğruluğu sonsuza dek kalıcıdır, Gücü ve saygınlığı artar.
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
Kötü kişi bunu görünce kudurur, Dişlerini gıcırdatır, kendi kendini yer, bitirir. Kötülerin dileği boşa çıkar.