< Masalimo 112 >

1 Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
Bienaventurado el varón que teme a Jehová: en sus mandamientos se deleita en gran manera:
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
Su simiente será valiente en la tierra: la generación de los rectos será bendita.
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Hacienda y riquezas habrá en su casa; y su justicia permanece para siempre.
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
Resplandeció en las tinieblas luz a los rectos: clemente, y misericordioso, y justo.
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
El buen varón tiene misericordia, y presta: gobierna sus cosas con juicio.
6 Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
Por lo cual para siempre no resbalará: en memoria eterna será el justo:
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
De mala fama no tendrá temor: su corazón está aparejado, confiado en Jehová.
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
Asentado está su corazón, no temerá, hasta que vea en sus enemigos la venganza.
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
Esparce, da a los pobres, su justicia permanece para siempre; su cuerno será ensalzado en gloria.
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
El impío verá, y airarse ha: sus dientes crujirá, y carcomerse ha: el deseo de los impíos perecerá.

< Masalimo 112 >