< Masalimo 112 >

1 Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
Благо човеку који се боји Господа, коме су веома омилеле заповести Његове.
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
Силно ће бити на земљи семе његово, род праведнички биће благословен.
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Обиље је и богатство у дому његовом, и правда његова траје довека.
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
У тами сјаје видело праведницима од доброг, милостивог и праведног.
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
Благо ономе који је милостив и даје у зајам! Он ће дати тврђу речима својим на суду.
6 Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
Јер неће посрнути довека, праведник ће се спомињати увек.
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
Не боји се злог гласа; срце је његово стално, узда се у Господа.
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
Утврђено је срце његово, неће се побојати, и видеће како падају непријатељи његови.
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
Просипа, даје убогима; правда његова траје довека, рог се његов узвишује у слави.
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
Безбожник види, и једи се, шкргуће зубима својим, и сахне. Жеља ће безбожницима пропасти.

< Masalimo 112 >