< Masalimo 112 >
1 Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
MEID pai ol o me majak Ieowa, me kin peren kola a kujoned akan.
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
Kadaudok a pan kelail nan jap o; kainok en me melel akan pan pwaida.
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Im a pan dir en dipijou melel o a pun pan potopot eta.
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
Marain kin daka dan me melel akan nan waja rotorot, a kin dir en mak o kalanan o pun.
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
Meid pai ol o me kalanan, o kin kijakija wei; a pan pwaida ni anjaun kadeik.
6 Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
Pwe a jota pan luetala kokolata; me pun amen iei men kataman joutuk eu.
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
A jota pan majak ron jued monion i me kelail ni a kaporoporeki Ieowa.
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
Monion i me kelail, a jota km majak, lao a pan peren kida a imwintiti kan.
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
A kin kamoredi o kijakij on me jamama kan; a pun pan potopot eta; oj a pan kokoda o indand mau.
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
Me doo jan Kot pan kilan ap makara kida; a pan teterokki ni akan ap joredi; inon en me doo jan Kot akan pan nikila.