< Masalimo 112 >

1 Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
Halleluja! Salig er den mann som frykter Herren, som har sin store lyst i hans bud.
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
Hans avkom skal være mektig på jorden; de opriktiges slekt skal velsignes.
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Det er velstand og rikdom i hans hus, og hans rettferdighet står fast evindelig.
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
Det går op et lys i mørket for de opriktige, for den som er nådig og barmhjertig og rettferdig.
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
Lykkelig er den mann som forbarmer sig og låner ut; han hevder all sin sak i dommen.
6 Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
For han skal ikke rokkes evindelig; den rettferdige skal være i evig minne.
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
Han skal ikke frykte for nogen ond tidende; hans hjerte er fast, det setter sin lit til Herren.
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
Hans hjerte er trygt; han frykter ikke, inntil han ser med lyst på sine fiender.
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
Han har strødd ut, han har gitt de fattige; hans rettferdighet står fast evindelig, hans horn skal ophøies med ære.
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
Den ugudelige skal se det og harmes, han skal skjære tenner og optæres; de ugudeliges attrå blir til intet.

< Masalimo 112 >