< Masalimo 112 >

1 Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
Alleluia, conversio Aggaei, et Zachariae. Beatus vir, qui timet Dominum: in mandatis eius volet nimis.
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
Potens in terra erit semen eius: generatio rectorum benedicetur.
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Gloria, et divitiae in domo eius: et iustitia eius manet in saeculum saeculi.
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
Exortum est in tenebris lumen rectis: misericors, et miserator, et iustus.
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
Iucundus homo qui miseretur et commodat, disponet sermones suos in iudicio:
6 Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
quia in aeternum non commovebitur.
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
In memoria aeterna erit iustus: ab auditione mala non timebit. Paratum cor eius sperare in Domino,
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
confirmatum est cor eius: non commovebitur donec despiciat inimicos suos.
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
Dispersit, dedit pauperibus: iustitia eius manet in saeculum saeculi, cornu eius exaltabitur in gloria.
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
Peccator videbit, et irascetur, dentibus suis fremet et tabescet: desiderium peccatorum peribit.

< Masalimo 112 >