< Masalimo 112 >

1 Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
Louez l'Eternel. [Aleph.] Bienheureux est l'homme qui craint l'Eternel, [Beth.] et qui prend un singulier plaisir en ses commandements!
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
[Guimel.] Sa postérité sera puissante en la terre, [ Daleth.] la génération des hommes droits sera bénie.
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
[ He.] Il y aura des biens et des richesses en sa maison; [Vau.] et sa justice demeure à perpétuité.
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
[Zaïn.] La lumière s'est levée dans les ténèbres à ceux qui sont justes; [Heth.] il est pitoyable, miséricordieux et charitable.
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
[Teth.] L'homme de bien fait des aumônes, et prête; [Jod.] Il dispense ses affaires avec droiture.
6 Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
[Caph.] Même il ne sera jamais ébranlé. [Lamed.] Le juste sera en mémoire perpétuelle.
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
[Mem.] Il n'aura peur d'aucun mauvais rapport; [Nun.] Son cœur est ferme s'assurant en l'Eternel.
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
[Samech.] Son cœur est bien appuyé, il ne craindra point, [Hajin.] jusqu’à ce qu'il ait vu en ses adversaires [ce qu'il désire].
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
[Pe.] Il a répandu, il a donné aux pauvres; [Tsade.] sa justice demeure à perpétuité; [Koph.] sa corne sera élevée en gloire.
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
[Resch.] Le méchant le verra, et en aura du dépit. [Sein.] Il grincera les dents, et se fondra; [Thau.] le désir des méchants périra.

< Masalimo 112 >