< Masalimo 112 >

1 Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
Halelujah. Blahoslavený muž, kterýž se bojí Hospodina, a v přikázaních jeho má velikou líbost.
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
Mocné na zemi bude símě jeho, rodina upřímých požehnání dojde.
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Zboží a bohatství v domě jeho, a spravedlnost jeho zůstává na věky.
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
Vzchází ve tmách světlo upřímým, milostivý jest, milosrdný a spravedlivý.
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
Dobrý člověk slitovává se i půjčuje, a řídí své věci s soudem.
6 Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
Nebo nepohne se na věky, v paměti věčné bude spravedlivý.
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
Slyše zlé noviny, nebojí se; stálé jest srdce jeho, a doufá v Hospodina.
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
Utvrzené srdce jeho nebojí se, až i uzří pomstu na svých nepřátelích.
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
Rozděluje štědře, a dává nuzným; spravedlnost jeho zůstává na věky, roh jeho bude vyvýšen v slávě.
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
Bezbožný vida to, zlobiti se, zuby svými škřipěti a schnouti bude; žádost bezbožníků zahyne.

< Masalimo 112 >