< Masalimo 112 >

1 Tamandani Yehova. Wodala munthu amene amaopa Yehova, amene amakondwera kwambiri ndi malamulo ake.
你们要赞美耶和华! 敬畏耶和华,甚喜爱他命令的, 这人便为有福!
2 Ana ake adzakhala amphamvu mʼdziko; mʼbado wa olungama mtima udzadalitsidwa.
他的后裔在世必强盛; 正直人的后代必要蒙福。
3 Kulemera ndi chuma zili mʼnyumba yake, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
他家中有货物,有钱财; 他的公义存到永远。
4 Ngakhale mu mdima kuwala kumatulukira olungama mtima; wokoma mtima, wachifundo ndi wowongoka mtima.
正直人在黑暗中,有光向他发现; 他有恩惠,有怜悯,有公义。
5 Zinthu zabwino zidzabwera kwa iye amene amapereka mowolowamanja ndi wokongoletsa mwaufulu, amene amachita ntchito yake mwachilungamo.
施恩与人、借贷与人的,这人事情顺利; 他被审判的时候要诉明自己的冤。
6 Ndithu sadzagwedezeka; munthu wolungama sadzayiwalika mpaka muyaya.
他永不动摇; 义人被记念,直到永远。
7 Saopa akamva zoyipa zimene zachitika; mtima wake ndi wokhazikika ndipo amadalira Yehova.
他必不怕凶恶的信息; 他心坚定,倚靠耶和华。
8 Mtima wake ndi wotetezedwa, sadzakhala ndi mantha; potsiriza pake adzayangʼana adani ake mwachipambano.
他心确定,总不惧怕, 直到他看见敌人遭报。
9 Wopereka mphatso zake mowolowamanja kwa osauka, chilungamo chake chimanka mpaka muyaya; nyanga yake idzakwezedwa mwaulemu.
他施舍钱财,周济贫穷; 他的仁义存到永远。 他的角必被高举,大有荣耀。
10 Munthu woyipa adzaona zimenezi ndipo adzapsa mtima; adzakukuta mano ake ndipo adzasungunuka. Zolakalaka za anthu oyipa sizidzachitika konse.
恶人看见便恼恨,必咬牙而消化; 恶人的心愿要归灭绝。

< Masalimo 112 >