< Masalimo 111 >
1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Dejen que que el Señor sea alabado. Alabaré al Señor con todo mi corazón, entre los rectos y en la reunión del pueblo.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
Las obras del Señor son grandes, buscadas por todos aquellos que se deleitan en ellas.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Su obra está llena de honor y gloria; y su justicia es inmutable para siempre.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
Cierto para siempre es el recuerdo de sus maravillas; el Señor está lleno de compasión y misericordia.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
Ha dado comida a sus adoradores; mantendrá su acuerdo en mente para siempre.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
Ha dejado en claro a su pueblo el poder de sus obras, dándoles la herencia de las naciones.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
Las obras de sus manos son fe y justicia; todas sus leyes son inmutables.
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
Pues son firmes por los siglos de los siglos, se hacen con fe y justicia.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
Él ha enviado salvación a su pueblo; él ha dado su palabra para siempre: santo es su nombre y grandemente temible.
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
El temor del Señor es la mejor parte de la sabiduría: todos los que guardan sus leyes son sabios: su alabanza es eterna.