< Masalimo 111 >

1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Лэудаць пе Домнул! Вой лэуда пе Домнул дин тоатэ инима мя, ын товэрэшия оаменилор фэрэ приханэ ши ын адунаре.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
Марь сунт лукрэриле Домнулуй, черчетате де тоць чей че ле юбеск!
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Стрэлучире ши мэрецие есте лукраря Луй, ши дрептатя Луй цине ын вечь!
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
Ел а лэсат о адучере аминте а минунилор Луй; Домнул есте ындурэтор ши милостив.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
Ел а дат хранэ челор че се тем де Ел; Ел Ышь адуче пуруря аминте де легэмынтул Луй.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
Ел а арэтат попорулуй Сэу путеря лукрэрилор Луй, кэч ле-а дат моштениря нямурилор.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
Лукрэриле мынилор Луй сунт крединчошие ши дрептате; тоате порунчиле Луй сунт адевэрате,
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
ынтэрите пентру вешничие, фэкуте ку крединчошие ши неприхэнире.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
А тримис попорулуй Сэу избэвиря, а ашезат легэмынтул Сэу ын вечь; Нумеле Луй есте сфынт ши ынфрикошат.
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
Фрика де Домнул есте ынчепутул ынцелепчуний; тоць чей че о пэзеск ау о минте сэнэтоасэ ши слава Луй цине ын вечь.

< Masalimo 111 >