< Masalimo 111 >
1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Halleluja. Będę wysławiał Pana całem sercem w radzie szczerych, i w zgromadzeniu.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
Wielkie sprawy Pańskie, jawne u wszystkich, którzy się w nich kochają.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Chwalebne i ozdobne dzieło jego, a sprawiedliwość jego trwa na wieki.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
Pamiątkę cudów swoich uczynił miłosierny a litościwy Pan.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
Dał pokarm tym, którzy się go boją, pamiętając wiecznie na przymierze swoje.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
Moc spraw swoich oznajmił ludowi swemu, dawszy im dziedzictwo pogan.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
Uczynki rąk jego prawda i sąd; nieodmienne są wszystkie przykazania jego,
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
Utwierdzone na wieki wieczne, uczynione w prawdzie i w szczerości.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
Wykupienie posławszy ludowi swemu, przykazał na wieki strzedź przymierza swego; święte i straszne jest imię jego.
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
Początek mądrości jest bojaźń Pańska; rozumu dobrego nabywają wszyscy, którzy rozkazanie Pańskie czyną; chwała jego trwa na wieki.