< Masalimo 111 >

1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Dumisani iNkosi! Ngizayibonga iNkosi ngenhliziyo yonke, emhlanganweni wabaqotho lebandleni.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
Mikhulu imisebenzi yeNkosi, idingwa yilabo abathokoza ngayo.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Ulodumo lenkazimulo umsebenzi wayo, lokulunga kwayo kumi kuze kube nininini.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
Yenzile izimangaliso zayo zikhunjulwe; iNkosi ilomusa lesihawu.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
Iyabapha ukudla labo abayesabayo; iyakhumbula kuze kube phakade isivumelwano sayo.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
Yazisile abantu bayo amandla emisebenzi yayo, ngokubanika ilifa lezizwe.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
Imisebenzi yezandla zayo iliqiniso lokwehlulela; imithetho yayo yonke iqinisekile.
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
Isekelwe kuze kube phakade laphakade, yenziwa ngeqiniso langobuqotho.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
Yathumela uhlengo ebantwini bayo; ilaye isivumelwano sayo kuze kube nininini; lingcwele liyesabeka ibizo layo.
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
Ukuyesaba iNkosi kuyikuqala kokuhlakanipha; balokuqedisisa okuhle bonke abayenzayo imilayo. Indumiso yayo imi kuze kube nininini.

< Masalimo 111 >