< Masalimo 111 >

1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Dumisani uThixo. Ngizambabaza uThixo ngenhliziyo yami yonke enkundleni yabaqotho lasemhlanganweni.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
Mikhulu imisebenzi kaThixo; isemicabangweni yabo bonke abathokoza ngayo.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Zilenkazimulo lobukhosi izenzo zakhe, lokulunga Kwakhe kumi kuze kube laphakade.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
Wenzile ukuthi izimanga zakhe zikhunjulwe; uThixo ulomusa lesihawu.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
Uyabapha ukudla labo abamesabayo; uyasikhumbula isivumelwano Sakhe lanini.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
Ubatshengisile abantu bakhe amandla emisebenzi yakhe, ngokubapha amazwe ezinye izizwe.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
Imisebenzi yezandla zakhe ithembekile, ilungile; zonke iziqondiso zakhe ziyathembeka.
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
Zimi kaziguquki nini lanini, zenziwa ngeqiniso langobuqotho.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
Wathumela abantu bakhe insindiso; wasingcwelisa isivumelwano Sakhe okwanininini lingcwele liyesabeka ibizo lakhe.
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
Ukumesaba uThixo kuyikuqala kwenhlakanipho bonke abalandela iziqondiso zakhe balokuzwisisa okuhle. Kungokwakhe ukudunyiswa kwaphakade.

< Masalimo 111 >