< Masalimo 111 >
1 Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
Pujilah TUHAN! Dengan segenap hati aku bersyukur kepada TUHAN di tengah himpunan umat-Nya.
2 Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
Sungguh ajaib perbuatan-perbuatan TUHAN, layak diselidiki oleh orang-orang yang menyukainya.
3 Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
Pekerjaan TUHAN agung dan terpuji, keadilan-Nya kekal abadi.
4 Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
TUHAN itu pengasih dan penyayang, Ia melakukan perbuatan-perbuatan yang mengagumkan, supaya kita tetap mengingatnya.
5 Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
Ia memberi rezeki kepada orang yang takwa, dan selalu ingat akan perjanjian-Nya.
6 Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
Ia telah menunjukkan kuasa-Nya kepada umat-Nya, dengan memberi mereka tanah pusaka bangsa-bangsa.
7 Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
TUHAN adil dan setia dalam segala tindakan-Nya, segala perintah-Nya dapat diandalkan.
8 Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
Hukum-Nya bertahan sepanjang masa, diberikan dalam kebenaran dan keadilan.
9 Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
Ia membebaskan umat-Nya, dan mengadakan perjanjian kekal dengan mereka. Dialah TUHAN yang kudus dan perkasa!
10 Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.
Barangsiapa ingin menjadi bijaksana harus menghormati TUHAN, Ia memberi pengertian kepada semua orang yang taat. Terpujilah TUHAN sepanjang masa!